Publicidade

Salmos 148

1 Tamandani Yehova.

Tamandani Yehova, inu a kumwamba,

mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.

2 Mutamandeni, inu angelo ake onse,

mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.

3 Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,

mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.

4 Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba

ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.

5 Zonse zitamande dzina la Yehova

pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.

6 Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;

analamula ndipo sizidzatha.

7 Tamandani Yehova pa dziko lapansi,

inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,

8 inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,

mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,

9 inu mapiri ndi zitunda zonse,

inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,

10 inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,

inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.

11 Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,

inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.

12 Inu anyamata ndi anamwali,

inu nkhalamba ndi ana omwe.

13 Onsewo atamande dzina la Yehova

pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;

ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.

14 Iye wakwezera nyanga anthu ake,

matamando a anthu ake onse oyera mtima,

Aisraeli, anthu a pamtima pake.

Tamandani Yehova.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-