Publicidade

Salmos 146

1 Tamandani Yehova.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.

3 Musamadalire mafumu,

anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.

4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;

zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.

5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi

Mulungu wa Yakobo.

6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;

Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.

7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa

ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Yehova amamasula amʼndende,

8 Yehova amatsekula maso anthu osaona,

Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,

Yehova amakonda anthu olungama.

9 Yehova amasamalira alendo

ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,

koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-