Publicidade

Salmos 1

1 Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake

ndipo masamba ake safota.

Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.

4 Sizitero ndi anthu oyipa!

Iwo ali ngati mungu

umene umawuluzidwa ndi mphepo.

5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,

kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,

koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-