Publicidade

Salmos 127

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.

1 Yehova akapanda kumanga nyumba,

omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.

Yehova akapanda kulondera mzinda,

mlonda akanangolondera pachabe.

2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa

ndi kusagona msanga madzulo,

kuvutikira chakudya choti mudye,

pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,

ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.

4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja

mwa munthu wankhondo.

5 Wodala munthu

amene motengera mivi mwake mwadzaza.

Iwo sadzachititsidwa manyazi

pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-