Publicidade

Salmos 120

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,

ndipo Iye amandiyankha.

2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,

ndi kwa anthu achinyengo.

3 Kodi adzakuchitani chiyani,

ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?

4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,

ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,

kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!

6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati

pa iwo amene amadana ndi mtendere.

7 Ine ndine munthu wamtendere;

koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_06-50-08-