Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 120

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,

ndipo Iye amandiyankha.

2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,

ndi kwa anthu achinyengo.

3 Kodi adzakuchitani chiyani,

ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?

4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,

ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,

kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!

6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati

pa iwo amene amadana ndi mtendere.

7 Ine ndine munthu wamtendere;

koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também