Publicidade

Salmos 118

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

2 Israeli anene kuti:

"Chikondi chake ndi chosatha."

3 Banja la Aaroni linene kuti,

"Chikondi chake ndi chosatha."

4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti:

"Chikondi chake ndi chosatha."

5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova,

ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.

6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha.

Munthu angandichite chiyani?

7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa.

Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.

8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova

kusiyana ndi kudalira munthu.

9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova

kusiyana ndi kudalira mafumu.

10 Anthu a mitundu yonse anandizinga,

koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

11 Anandizinga mbali zonse,

koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

12 Anandizinga ngati njuchi,

koma anatha msanga ngati moto wapaminga;

mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa,

koma Yehova anandithandiza.

14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.

15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano

ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti:

"Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!

16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba

Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!"

17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo

ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.

18 Yehova wandilanga koopsa,

koma sanandipereke ku imfa.

19 Tsekulireni zipata zachilungamo,

kuti ndifike kudzayamika Yehova.

20 Ichi ndicho chipata cha Yehova

chimene olungama mtima okha adzalowerapo.

21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha;

mwakhala chipulumutso changa.

22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana

wasanduka wapangodya;

23 Yehova ndiye wachita zimenezi

ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.

24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;

tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.

25 Inu Yehova, tipulumutseni;

Yehova, tipambanitseni.

26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova.

Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.

27 Yehova ndi Mulungu,

ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife.

Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu,

mpaka ku nyanga za guwa.

28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;

Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.

29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-