Publicidade

Salmos 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1 Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.

2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;

akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.

3 Iye akumbukire nsembe zako zonse

ndipo alandire nsembe zako zopsereza.

Sela

4 Akupatse chokhumba cha mtima wako

ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.

5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana

ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,

Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;

Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika

ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.

7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo

koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.

8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,

koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu!

Tiyankheni pamene tikuyitanani!

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-