Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 131

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.

1 Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,

maso anga siwonyada;

sinditengeteka mtima

ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.

2 Koma moyo wanga ndawutontholetsa

ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,

moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.

3 Yembekeza Yehova, iwe Israeli,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também