Publicidade

Salmos 3

Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu.

1 Inu Yehova, achulukadi adani anga!

Achulukadi amene andiwukira!

2 Ambiri akunena za ine kuti,

"Mulungu sadzamupulumutsa."

Sela

3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza,

Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.

4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula

ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera.

Sela

5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo;

ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.

6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene

abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.

7 Dzukani, Inu Yehova!

Pulumutseni, Inu Mulungu wanga.

Akantheni adani anga onse pa msagwada;

gululani mano a anthu oyipa.

8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.

Madalitso akhale pa anthu anu.

Sela

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-