Publicidade

Salmos 55

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

1 Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,

musakufulatire kupempha kwanga,

2 mverani ndipo mundiyankhe.

Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru

3 chifukwa cha mawu a adani anga,

chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;

pakuti andidzetsera masautso

ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;

mantha a imfa andigwera.

5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;

mantha aakulu andithetsa nzeru.

6 Ndinati, "Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!

Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.

7 Ndikanathawira kutali

ndi kukakhala mʼchipululu.

8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;

kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho."

9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;

pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.

10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;

nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.

11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;

kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine

ndikanapirira;

akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,

ndikanakabisala.

13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,

bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.

14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala

pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;

alowe mʼmanda ali amoyo

pakuti choyipa chili pakati pawo.

16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,

ndipo Yehova anandipulumutsa.

17 Madzulo, mmawa ndi masana

ndimalira mowawidwa mtima,

ndipo Iye amamva mawu anga.

18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa

pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,

ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.

19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,

adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,

chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa

ndipo saopa Mulungu.

20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;

iye akuphwanya pangano ake.

21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala

komabe nkhondo ili mu mtima mwake;

mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,

komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.

22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova

ndipo Iye adzakulimbitsani;

Iye sadzalola kuti wolungama agwe.

23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa

kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;

anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo

sadzakhala moyo theka la masiku awo,

koma ine ndimadalira Inu.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-