Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 43

1 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2 Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3 Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4 Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também