Publicidade

Salmos 61

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

1 Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;

mvetserani pemphero langa.

2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu

ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;

tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.

3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,

nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya

ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.

5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;

mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,

zaka zake kwa mibado yochuluka.

7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;

ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu

ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-