Publicidade

Salmos 112

1 Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,

amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;

mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;

wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,

amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

6 Ndithu sadzagwedezeka;

munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;

mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.

8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;

potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;

nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;

adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.

Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-