Publicidade

Salmos 32

Salimo la Davide. Malangizo.

1 Ngodala munthu

amene zolakwa zake zakhululukidwa;

amene machimo ake aphimbidwa.

2 Ngodala munthu

amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye

ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.

3 Pamene ndinali chete,

mafupa anga anakalamba

chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.

4 Pakuti usana ndi usiku

dzanja lanu linandipsinja;

mphamvu zanga zinatha

monga nthawi yotentha yachilimwe.

Sela

5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu,

sindinabise mphulupulu zanga.

Ndinati, "Ine ndidzawulula

zolakwa zanga kwa Yehova,

ndipo Inu munandikhululukira

mlandu wa machimo anga."

Sela

6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo

pomwe mukupezeka;

ndithu pamene madzi amphamvu auka,

sadzamupeza.

7 Inu ndi malo anga obisala;

muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga

ndi nyimbo zachipulumutso.

Sela

8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo;

ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.

9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu,

zimene zilibe nzeru,

koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu,

ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.

10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa

koma chikondi chosatha cha Yehova

chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.

11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama;

imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-