Publicidade

Salmos 82

Salimo la Asafu.

1 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;

Iye akuweruza pakati pa "milungu."

2 "Mudzateteza osalungama mpaka liti,

ndi kukondera anthu oyipa?

3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;

mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;

apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

5 "Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.

Amayendayenda mu mdima;

maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6 "Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,

nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’

7 Koma mudzafa ngati anthu wamba;

mudzagwa ngati wolamula wina aliyense."

8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,

pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-