Publicidade

Salmos 67

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.

1 Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,

achititse kuti nkhope yake itiwalire.

2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,

chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.

3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,

pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo

ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.

5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

6 Nthaka yabereka zokolola zake;

tidalitseni Mulungu wathu.

7 Mulungu atidalitse

kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-