Publicidade

Salmos 125

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,

limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu,

momwemonso Yehova azungulira anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala

pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,

kuti anthu olungamawo

angachite nawonso zoyipa.

4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,

amene ndi olungama mtima

5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-