Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 114

1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto,

nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,

2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu,

Israeli anasanduka ufumu wake.

3 Nyanja inaona ndi kuthawa,

mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;

4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna,

timapiri ngati ana ankhosa.

5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa?

iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?

6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna,

inu timapiri, ngati ana ankhosa?

7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi,

pamaso pa Mulungu wa Yakobo,

8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime,

thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também