Publicidade

Salmos 23

Salimo la Davide.

1 Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

2 Amandigoneka pa msipu wobiriwira,

amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,

3 amatsitsimutsa moyo wanga.

Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo

chifukwa cha dzina lake.

4 Ngakhale ndiyende

mʼchigwa cha mdima wakuda bii,

sindidzaopa choyipa,

pakuti Inu muli ndi ine;

chibonga chanu ndi ndodo yanu

zimanditonthoza.

5 Mumandikonzera chakudya

adani anga akuona.

Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta;

chikho changa chimasefukira.

6 Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata

masiku onse a moyo wanga,

ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova

kwamuyaya.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-