Publicidade

Salmos 93

1 Yehova akulamulira, wavala ulemerero;

Yehova wavala ulemerero ndipo wadzimangirira mphamvu,

dziko lonse lakhazikika kolimba; silingasunthidwe.

2 Mpando wanu waufumu unakhazikika kalekale;

Inu ndinu wamuyaya.

3 Nyanja zakweza Inu Yehova,

nyanja zakweza mawu ake;

nyanja zakweza mafunde ake ochita mkokomo.

4 Yehova ndi wamphamvu kupambana mkokomo wa madzi ambiri,

ndi wamphamvu kupambana mafunde a nyanja,

Yehova mmwamba ndi wamphamvu.

5 Malamulo anu Yehova ndi osasinthika;

chiyero chimakongoletsa nyumba yanu

mpaka muyaya.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_06-50-08-