Publicidade

Salmos 84

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Gititi. Salimo la ana a Kora.

1 Malo anu okhalamo ndi okomadi,

Inu Yehova Wamphamvuzonse!

2 Moyo wanga ukulakalaka, mpaka kukomoka,

kufuna mabwalo a Yehova;

Mtima wanga ndi thupi langa zikufuwulira

Mulungu wamoyo.

3 Ngakhale timba wapeza nyumba yokhalamo,

ndiponso namzeze wadzipezera yekha chisa,

kumene amagonekako ana ake

pafupi ndi guwa lanu la nsembe,

Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga.

4 Odala amene amakhala mʼNyumba yanu;

nthawi zonse amakutamandani.

Sela

5 Odala amene mphamvu yawo ili mwa Inu,

mitima yawo ikufunitsitsa kuyenda mʼmisewu yopita ku Ziyoni.

6 Pamene akudutsa chigwa cha Baka,

amachisandutsa malo a akasupe;

mvula ya chizimalupsa imadzazanso mayiwe ake.

7 Iwo amanka nakulirakulira mphamvu

mpaka aliyense ataonekera pamaso pa Mulungu mu Ziyoni.

8 Imvani pemphero langa, Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse;

mvereni Inu Mulungu wa Yakobo.

Sela

9 Yangʼanani chishango chathu, Inu Mulungu;

yangʼanani mokoma mtima pa wodzozedwa wanu.

10 Nʼkwabwino kukhala mʼmabwalo anu tsiku limodzi

kuposa kukhala kwina kwake kwa zaka 1,000;

Ine ndingakonde kukhala mlonda wa pa khomo la Nyumba ya Mulungu wanga

kuposa kukhala mʼmatenti a anthu oyipa.

11 Pakuti Yehova Mulungu ndi dzuwa ndi chishango;

Yehova amapereka chisomo ndi ulemu;

Iye sawamana zinthu zabwino

iwo amene amayenda mwangwiro.

12 Inu Yehova Wamphamvuzonse,

wodala ndi munthu amene amakhulupirira Inu.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-