Publicidade

Salmos 50

Salimo la Asafu.

1 Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,

akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi

kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.

2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri

Mulungu akuwala.

3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;

moto ukunyeketsa patsogolo pake,

ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho

4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga

ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.

5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,

amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.

6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,

pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.

7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,

iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;

ndine Mulungu, Mulungu wako.

8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,

kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.

9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako

kapena mbuzi za mʼkhola lako,

10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga

ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.

11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri

ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.

12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani,

pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.

13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna

kapena kumwa magazi a mbuzi?

14 "Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu,

kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.

15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso;

Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza."

16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti,

"Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga

kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?

17 Iwe umadana ndi malangizo anga

ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.

18 Ukaona wakuba umamutsatira,

umachita maere ako pamodzi ndi achigololo

19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa

ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.

20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako

ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.

21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete;

umaganiza kuti ndine wofanana nawe

koma ndidzakudzudzula

ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.

22 "Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu

kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:

23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,

ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse

chipulumutso cha Mulungu."

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_06-50-08-