Publicidade

Salmos 123

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Ndikweza maso anga kwa Inu,

kwa Inu amene mumakhala kumwamba.

2 Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo,

monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake,

choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu,

mpaka atichitire chifundo.

3 Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo,

pakuti tapirira chitonzo chachikulu.

4 Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza,

chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-