Publicidade

Salmos 8

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide.

1 Inu Yehova Ambuye athu,

dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu

mʼmayiko onse akumwamba.

2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda,

Inu mwakhazikitsa mphamvu

chifukwa cha adani anu,

kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.

3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba,

ntchito ya zala zanu,

mwezi ndi nyenyezi,

zimene mwaziyika pa malo ake,

4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira,

ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?

5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba

ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.

6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu;

munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;

7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi

ndi nyama zakuthengo,

8 mbalame zamlengalenga

ndi nsomba zamʼnyanja

zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.

9 Inu Yehova, Ambuye athu,

dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-