Publicidade

Salmos 149

1 Tamandani Yehova.

Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.

2 Israeli asangalale mwa mlengi wake;

anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.

3 Atamande dzina lake povina

ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.

4 Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake;

Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.

5 Oyera mtima asangalale mu ulemu wake

ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.

6 Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo,

ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,

7 kubwezera chilango anthu a mitundu ina,

ndi kulanga anthu a mitundu yonse,

8 kumanga mafumu awo ndi zingwe,

anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,

9 kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo

Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.

Tamandani Yehova.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-