Publicidade

Salmos 4

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide.

1 Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu,

Inu Mulungu wa chilungamo changa.

Pumulitseni ku zowawa zanga;

chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.

2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi?

Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza?

Sela.

3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika;

Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.

4 Kwiyani koma musachimwe;

pamene muli pa mabedi anu,

santhulani mitima yanu ndi kukhala chete.

Sela

5 Perekani nsembe zolungama

ndipo dalirani Yehova.

6 Ambiri akufunsa kuti, "Ndani angationetse chabwino chilichonse?"

Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.

7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu

kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.

8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere,

pakuti Inu nokha, Inu Yehova,

mumandisamalira bwino.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-