Publicidade

Salmos 13

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1 Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?

Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?

2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga

ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?

Mpaka liti adani anga adzandipambana?

3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.

Walitsani maso anga kuti ndingafe;

4 mdani wanga adzati, "Ndamugonjetsa,"

ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.

5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;

mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.

6 Ine ndidzayimbira Yehova

pakuti wandichitira zokoma.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-