Publicidade

Salmos 124

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,

anene tsono Israeli,

2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,

potiwukira anthuwo,

3 iwo atatipsera mtima,

akanatimeza amoyo;

4 chigumula chikanatimiza,

mtsinje ukanatikokolola,

5 madzi a mkokomo

akanatikokolola.

6 Atamandike Yehova,

amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.

7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame

yokodwa mu msampha wa mlenje;

msampha wathyoka,

ndipo ife tapulumuka.

8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_18-40-07-