Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 150

1 Tamandani Yehova.

Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika;

mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.

2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu;

mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.

3 Mutamandeni poyimba malipenga,

mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.

4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina,

mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.

5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga,

mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.

6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova.

Tamandani Yehova.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também