Publicidade

Salmos 6

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide.

1 Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

kapena kundilanga mu ukali wanu.

2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka;

Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.

3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu.

Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?

4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse;

pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira;

Amakutamandani ndani ali ku manda?

6 Ine ndatopa ndi kubuwula;

usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga;

ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.

7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni;

akulephera kuona chifukwa cha adani anga.

8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa,

pakuti Yehova wamva kulira kwanga.

9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo;

Yehova walandira pemphero langa.

10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha;

adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-