Publicidade

Salmos 113

1 Tamandani Yehova.

Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

tamandani dzina la Yehova.

2 Yehova atamandidwe,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake,

dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.

4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse,

ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.

5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu,

Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?

6 amene amawerama pansi kuyangʼana

miyamba ndi dziko lapansi?

7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi

ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;

8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu,

pamodzi ndi mafumu a anthu ake.

9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake

monga mayi wa ana wosangalala.

Tamandani Yehova.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-