Publicidade

Salmos 130

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;

2 Ambuye imvani mawu anga.

Makutu anu akhale tcheru kumva

kupempha chifundo kwanga.

3 Inu Yehova, mukanamawerengera machimo,

Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?

4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro;

nʼchifukwa chake mumaopedwa.

5 Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera,

ndipo ndimakhulupirira mawu ake.

6 Moyo wanga umayembekezera Ambuye,

kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,

inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,

7 Yembekeza Yehova, iwe Israeli,

pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika

ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.

8 Iye mwini adzawombola Israeli

ku machimo ake onse.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-