Publicidade

Salmos 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Ndikweza maso anga ku mapiri;

kodi thandizo langa limachokera kuti?

2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3 Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli

sadzawodzera kapena kugona.

5 Yehova ndiye amene amakusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.

6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,

kapena mwezi nthawi ya usiku.

7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;

adzasunga moyo wako.

8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-16_06-50-08-