Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 128

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Odala ndi onse amene amaopa Yehova,

amene amayenda mʼnjira zake.

2 Udzadya chipatso cha ntchito yako;

madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka

mʼkati mwa nyumba yako;

ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi

kuzungulira tebulo lako.

4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa

amene amaopa Yehova.

5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni

masiku onse a moyo wako;

uwone zokoma za Yerusalemu,

6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também