Publicidade

Oséias 7

1 Pamene ndichiritsa Israeli,

machimo a Efereimu amaonekera poyera

ndiponso milandu ya Samariya sibisika.

Iwo amachita zachinyengo,

mbala zimathyola nyumba,

achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.

2 Koma sazindikira kuti Ine

ndimakumbukira zoyipa zawo zonse.

Azunguliridwa ndi zolakwa zawo;

ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.

3 "Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo,

akalonga amasekerera mabodza awo.

4 Onsewa ndi anthu azigololo,

otentha ngati moto wa mu uvuni,

umene wophika buledi sasonkhezera

kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.

5 Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu

akalonga amaledzera ndi vinyo,

ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.

6 Mitima yawo ili ngati uvuni;

amayandikira Mulungu mwachiwembu.

Ukali wawo umanyeka usiku wonse,

mmawa umayaka ngati malawi a moto.

7 Onsewa ndi otentha ngati uvuni,

amapha olamulira awo.

Mafumu awo onse amagwa,

ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.

8 "Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena;

Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.

9 Alendo atha mphamvu zake,

koma iye sakuzindikira.

Tsitsi lake layamba imvi

koma iye sakudziwa.

10 Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa,

koma pa zonsezi

iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake

kapena kumufunafuna.

11 "Efereimu ali ngati nkhunda

yopusa yopanda nzeru.

Amayitana Igupto

namapita ku Asiriya.

12 Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga;

ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga.

Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi

ndidzawakola.

13 Tsoka kwa iwo,

chifukwa andisiya Ine!

Chiwonongeko kwa iwo,

chifukwa andiwukira!

Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa

koma amayankhula za Ine monama.

14 Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima,

koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo.

Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano,

koma amandifulatira.

15 Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa,

koma amandikonzera chiwembu.

16 Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba;

ali ngati uta woonongeka.

Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga

chifukwa cha mawu awo achipongwe.

Motero iwo adzasekedwa

mʼdziko la Igupto.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-