Publicidade

Oséias 8

Israeli Akolola Kamvuluvulu

1 "Ika lipenga pakamwa pako.

Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova

chifukwa anthu aphwanya pangano langa

ndiponso agalukira lamulo langa.

2 Israeli akulirira kwa Ine kuti,

‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’

3 Koma Israeli wakana zabwino;

mdani adzamuthamangitsa.

4 Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga.

Amasankha akalonga popanda chilolezo changa.

Amadzipangira mafano

asiliva ndi agolide

koma adzawonongeka nawo.

5 Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe!

Mkwiyo wanga wayakira anthuwo.

Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?

6 Mafanowa ndi ochokera ku Israeli!

Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso;

si Mulungu amene anamupanga.

Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa,

mwana wangʼombe wa ku Samariya.

7 "Aisraeli amadzala mphepo

ndipo amakolola kamvuluvulu.

Tirigu alibe ngala;

sadzabala chakudya.

Akanabala chakudya

alendo akanadya chakudyacho.

8 Israeli wamezedwa,

tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina

ngati chinthu cha chabechabe.

9 Pakuti iwo anapita ku Asiriya

ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha.

Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.

10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu,

Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi.

Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa

ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.

11 "Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo,

maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.

12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga,

koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.

13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine

ndipo iwo amadya nyamayo,

koma Yehova sakondwera nazo.

Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo

ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo:

iwowo adzabwerera ku Igupto.

14 Israeli wayiwala Mlengi wake

ndipo wamanga nyumba zaufumu;

Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga.

Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo,

moto umene udzatenthe malinga awo."

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-