Publicidade

Salmos 25

Salimo la Davide.

1 Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.

2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga.

Musalole kuti ndichite manyazi

kapena kuti adani anga andipambane.

3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye

sadzachititsidwa manyazi

koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi

ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.

4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova,

phunzitseni mayendedwe anu;

5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa,

pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga,

ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.

6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu,

pakuti ndi zakalekale.

7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga

ndi makhalidwe anga owukira;

molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine,

pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.

8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama;

choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.

9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama

ndipo amawaphunzitsa njira zake.

10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika

kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.

11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova,

khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.

12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova?

Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.

13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse,

ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.

14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa;

amawulula pangano lake kwa iwowo.

15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse,

pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.

16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima,

pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.

17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira;

masuleni ku zowawa zanga.

18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga

ndipo mufafanize machimo anga onse.

19 Onani mmene adani anga achulukira

ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.

20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa;

musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndimathawira kwa Inu.

21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze,

chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.

22 Wombolani Israeli Inu Mulungu,

ku mavuto ake onse!

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-