Publicidade

Salmos 101

Salimo la Davide.

1 Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama;

kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.

2 Ndidzatsata njira yolungama;

nanga mudzabwera liti kwa ine?

Ndidzayenda mʼnyumba mwanga

ndi mtima wosalakwa.

3 Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa

pamaso panga.

Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro;

iwo sadzadziphatika kwa ine.

4 Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine;

ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.

5 Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri

ameneyo ndidzamuletsa;

aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza,

ameneyo sindidzamulekerera.

6 Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko,

kuti akhale pamodzi ndi ine;

iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa

adzanditumikira.

7 Aliyense wochita chinyengo

sadzakhala mʼnyumba mwanga.

Aliyense woyankhula mwachinyengo

sadzayima pamaso panga.

8 Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu

onse oyipa mʼdziko;

ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa

mu mzinda wa Yehova.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-