Publicidade

Salmos 14

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1 Chitsiru chimati mu mtima mwake,

"Kulibe Mulungu."

Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;

palibe amene amachita zabwino.

2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi,

kuyangʼana anthu onse

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

amene amafunafuna Mulungu.

3 Onse atembenukira kumbali,

onse pamodzi asanduka oyipa;

palibe amene amachita zabwino,

palibiretu ndi mmodzi yemwe.

4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?

Akudya anthu anga ngati chakudya chawo

ndipo satamanda Yehova?

5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,

pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.

6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,

koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.

7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!

Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,

Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-