Publicidade

Salmos 138

Salimo la Davide.

1 Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa "milungu."

2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera

ndipo ndidzayamika dzina lanu

chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,

pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu

kupambana zinthu zonse.

3 Pamene ndinayitana, munandiyankha;

munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.

4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,

pamene amva mawu a pakamwa panu.

5 Iwo ayimbe za njira za Yehova,

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,

koma anthu onyada amawadziwira chapatali.

7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,

mumasunga moyo wanga;

mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,

mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.

8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;

chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha

musasiye ntchito ya manja anu.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-