Publicidade

Salmos 24

Salimo la Davide.

1 Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo,

dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;

2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja

ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.

3 Ndani angakwere phiri la Yehova?

Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?

4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera,

amene sapereka moyo wake kwa fano

kapena kulumbira mwachinyengo.

5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova

ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.

6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova;

amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo.

Sela

7 Tukulani mitu yanu inu zipata;

tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,

kuti Mfumu yaulemerero ilowe.

8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?

Yehova Wamphamvuzonse,

Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.

9 Tukulani mitu yanu, inu zipata;

tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,

kuti Mfumu yaulemerero ilowe.

10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?

Yehova Wamphamvuzonse,

Iye ndiye Mfumu yaulemerero.

Sela

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-