4 Pilato anatulukanso ndipo anati kwa Ayuda, "Taonani, ine ndikumubweretsa kuti inu mudziwe kuti ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu." 5 Pamenepo Yesu anatuluka atavala nkhata yaminga ndi mkanjo wapepo ndipo Pilato anawawuza kuti, "Nayu munthu uja!"
6 Atangomuona Iye akulu a ansembe ndi akuluakulu ena anafuwula kuti, "Mpachikeni! Mpachikeni!"
Koma Pilato anayankha kuti, "Inu mutengeni ndi kumupachika. Koma ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu."