5 Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, "Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo." Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.