8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake,
koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Iye amaphimba mwezi wowala,
amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta,
kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.