40 Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, "Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi? 41 Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu."
42 Kenaka anati, "Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu."
43 Yesu anayankha kuti, "Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso."