Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru
20 Nzeru ikufuwula mu msewu,
ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu,
ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 "Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?
Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?
Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo.
Ine ndikukuwuzani maganizo anga
ndi kukudziwitsani mawu anga.