14Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’
25Kenaka Barnaba anapita ku Tarisisi kukafuna Saulo,
26ndipo pamene anamupeza anabwera naye ku Antiokeya. Barnaba ndi Saulo anasonkhana ndi mpingo kwa chaka chimodzi naphunzitsa anthu ambirimbiri. Okhulupirirawo anayamba kutchedwa Akhristu ku Antiokeya.
2Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
3Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,nkhata ya maluwa yokongolamʼmalo mwa phulusa,ndiwapatse mafuta achikondwereromʼmalo mwa kulira.Ndiwapatse chovala cha matamandomʼmalo mwa mtima wopsinjika.Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,yoyidzala Yehovakuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
10Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.