7 "Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova,
amene amatsamira pa Iye.
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi
umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje.
Mtengowo suopa pamene kukutentha;
masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse.
Suchita mantha pa chaka cha chilala
ndipo sulephera kubereka chipatso."