Publicidade

Jeremias 18

Ku Nyumba ya Wowumba Mbiya

1 Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2 "Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga." 3 Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero. 4 Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.

5 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, 6 "Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?" akutero Yehova. "Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-