6 Undiyike pamtima pako ngati chidindo,
ngati chidindo cha pa dzanja lako;
pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,
nsanje ndiyaliwuma ngati manda.
Chikondi chimachita kuti lawilawi
ngati malawi a moto wamphamvu.
7 Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,
mitsinje singachikokolole chikondicho.
Ngati wina apereka chuma chonse
cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,
adzangonyozeka nazo kotheratu.
Abwenzi